< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Sølvet har jo sit Leje, som renses, sit sted
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Jern hentes op af Jorden, og Sten smeltes om til Kobber.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
På Mørket gør man en Ende og ransager indtil de dybeste Kroge Mørkets og Mulmets Sten;
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
man bryder en Skakt under Foden, og glemte, foruden Fodfæste, hænger de svævende fjernt fra Mennesker.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
Af Jorden fremvokser Brød, imedens dens Indre omvæltes som af Ild;
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
i Stenen der sidder Safiren, og der er Guldstøv i den.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
Stien derhen er Rovfuglen ukendt, Falkens Øje udspejder den ikke;
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
den trædes ikke af stolte Vilddyr, Løven skrider ej frem ad den.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
På Flinten lægger man Hånd og omvælter Bjerge fra Roden;
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
i Klipperne hugger man Gange, alskens Klenodier skuer Øjet;
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
man tilstopper Strømmenes Kilder og bringer det skjulte for Lyset.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Men Visdommen - hvor mon den findes, og hvor er Indsigtens Sted?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Mennesket kender ikke dens Vej, den findes ej i de levendes Land;
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
Dybet siger: "I mig er den ikke!" Havet: "Ej heller hos mig!"
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
Man får den ej for det fineste Guld, for Sølv kan den ikke købes,
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
den opvejes ikke med Ofirguld, med kostelig Sjoham eller Safir;
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Guld og Glar kan ej måle sig med den, den fås ej i Bytte for gyldne Kar,
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
Krystal og Koraller ikke at nævne. At eje Visdom er mere end Perler,
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
Ætiopiens Topas kan ej måle sig med den, den opvejes ej med det rene Guld.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Men Visdommen - hvor mon den kommer fra, og hvor er Indsigtens Sted?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Den er dulgt for alt levendes Øje og skjult for Himmelens Fugle;
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Afgrund og Død må sige: "Vi hørte kun tale derom."
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
Gud er kendt med dens Vej, han ved, hvor den har sit Sted;
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
thi han skuer til Jordens Ender, alt under Himmelen ser han.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
Dengang han fastsatte Vindens Vægt og målte Vandet med Mål,
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
da han satte en Lov for Regnen, afmærked Tordenskyen dens Vej,
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
da skued og mønstred han den, han stilled den op og ransaged den.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
Men til Mennesket sagde han: "Se, HERRENs Frygt, det er Visdom, at sky det onde er Indsigt."

< Yobu 28 >