< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Máť zajisté stříbro prameny své, a zlato místo k přehánění.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Železo z země vzato bývá, a kámen rozpuštěný dává měď.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
Cíl ukládá temnostem, a všelikou dokonalost člověk vystihá, kámen mrákoty a stínu smrti.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
Protrhuje se řeka na obyvatele, tak že ji nemůže žádný přebřesti, a svozována bývá uměním smrtelného člověka, i odchází.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
Z země vychází chléb, ačkoli pod ní jest něco rozdílného, podobného k ohni.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
V některé zemi jest kamení zafirové a prach zlatý,
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
K čemuž stezky nezná žádný pták, aniž ji spatřilo oko luňáka,
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
Kteréž nešlapala mladá zvěř, aniž šel po ní lev.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
K škřemeni vztahuje ruku svou, a z kořene převrací hory.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
Z skálí vyvodí potůčky, a všecko, což jest drahého, spatřuje oko jeho.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
Vylévati se řekám zbraňuje, a tak cožkoli skrytého jest, na světlo vynáší.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Ale moudrost kde nalezena bývá? A kde jest místo rozumnosti?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Neví smrtelný člověk ceny její, aniž bývá nalezena v zemi živých.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
Propast praví: Není ve mně, moře také dí: Není u mne.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
Nedává se zlata čistého za ni, aniž odváženo bývá stříbro za směnu její.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
Nemůže býti ceněna za zlato z Ofir, ani za onychin drahý a zafir.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Nevrovná se jí zlato ani drahý kámen, aniž směněna býti může za nádobu z ryzího zlata.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
Korálů pak a perel se nepřipomíná; nebo nabytí moudrosti dražší jest nad klénoty.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
Není jí rovný v ceně smaragd z Mouřenínské země, aniž za čisté zlato může ceněna býti.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Odkudž tedy moudrost přichází? A kde jest místo rozumnosti?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Poněvadž skryta jest před očima všelikého živého, i před nebeským ptactvem ukryta jest.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Zahynutí i smrt praví: Ušima svýma slyšely jsme pověst o ní.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
Sám Bůh rozumí cestě její, a on ví místo její.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
Nebo on končiny země spatřuje, a všecko, což jest pod nebem, vidí,
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
Tak že větru váhu dává, a vody v míru odvažuje.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
On též vyměřuje dešti právo, i cestu blýskání hromů.
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
Hned tehdáž viděl ji, a rozhlásil ji, připravil ji, a vystihl ji.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
Èlověku pak řekl: Aj, bázeň Páně jest moudrost, a odstoupiti od zlého rozumnost.

< Yobu 28 >