< Yobu 27 >
1 Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
A OLELO hou mai la o Ioba i kana olelonane, i mai la,
2 “Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
Ma ke ola o ke Akua, nana i lawe aku kuu pono; A ma ka Mea mana, nana i hooawahia kuu uhane;
3 nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
I ka manawa a pau o kuu hanu iloko o'u, A o ke ola o ke Akua iloko o kuu mau puka ihu;
4 pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
Aole e olelo kuu lehelehe i ka hewa, A o kuu elelo aole e hoike aku i ka wahahee.
5 Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
Aole loa wau e hoapono aku ia oukou, a make au; Aole owau e lawe aku i kuu pono mai o'u aku la.
6 Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
Ma kuu pono ke hoopaa nei au, aole au e hookuu aku; Aole e hoino mai ia'u kuu naau i kekahi o kuu mau la.
7 “Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
E hoohalikeia kuu enemi me ka mea hewa, A o ka mea ku e mai ia'u me he mea pono ole la.
8 Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
No ka mea, heaha ka manaelana o ka aia, i ka wa e hoopau ai ia ia, I ku wa e kaili aku ai ke Akua i kona uhane?
9 Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
E hoolohe mai anei ke Akua i kona auwe ana, I ka manawa e hiki mai ai ka popilikia maluna ona?
10 Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
E hauoli anei ia i ka Mea mana? E kahea mau loa anei ia i ke Akua?
11 “Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
E ao aku au ia oukou ma ka lima o ke Akua: Aole au e huna i ka mea me ka Mea mana.
12 Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
Aia hoi, o oukou a pau, ua hoomaopopo oukou ia; No ke aha la oukou i manao lapuwale ai pela?
13 “Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
Eia ka uku no ke kanaka hewa imua o ke Akua, O ka hooilina a ka poe hookaumaha e loaa'i, mai ka Mea mana mai.
14 Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
Ina e hoonuiia kana poe keiki, no ka pahikaua no; A o kana poe mamo, aole e maona i ka berena.
15 Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
O kona poe e koe ana, e kanuia i ka make: Aole hoi e kanikau kana mau wahinekanemake.
16 Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
Ina e hoiliili oia i ke kala e like me ka lepo, A e hoomakaukau i ka lolekomo e like me ka palolo;
17 zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
E hoomakaukau no, aka, na ka mea pono e hookomo, A o ke kala, na ka mea hala ole e puunaue.
18 Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
Kukulu no ia i kona hale me he mu la, A e like me ke kamala a ke kiai i hana'i.
19 Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
Moe iho ilalo ka mea waiwai, aole e kanuia; Wehe ae ia i kona maka, aole iho la ia.
20 Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
Kau mai la na weliweli ia ia, e like me na wai, I ka po, lawe aku ka puahiohio ia ia.
21 Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
Na ka makani hikina ia e lawe aku, a hele aku ia, A o ka ino e lawe ia ia mai kona wahi aku.
22 Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
E hoolei aku [ke Akua] ia ia, aole ia e minamina: I ka holo ana, e holo no ia mai kona lima aku.
23 Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”
E pai lakou i ko lakou lima ia ia, A e kipaku ia ia mai kona wahi aku.