< Yobu 27 >

1 Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Alò, Job te kontinye diskou li. Li te di:
2 “Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
Kon Bondye viv la, ki te retire dwa m, Toupwisanki te fè m gen nanm anmè a,
3 nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
paske tan lavi toujou nan mwen. Souf Bondye la nan nen m.
4 pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
Lèv mwen, anverite, p ap pale sa ki pa dwat, ni lang mwen pa p pale manti.
5 Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
Fòk se lwen m pou m ta bay ou rezon. Jiskaske m mouri, mwen p ap lage entegrite m.
6 Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
Mwen kenbe fèm a ladwati mwen. Mwen p ap lage l menm. Kè m pa repwoche m depi gen lavi ladan m.
7 “Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
“Kite lènmi m kapab tankou mechan a. Kite sila ki leve kont mwen, san jistis.
8 Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
Paske ki espwa sila ki san Bondye a genyen lè l koupe retire nèt, lè Bondye fè l oblije bay lavi li?
9 Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
Èske Bondye va tande kri li lè malè rive li?
10 Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
Èske li va pran plezi nan Toupwisan an? Èske li va rele non Bondye a nan tout tan sa yo?
11 “Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
Mwen va enstwi ou nan pwisans Bondye. Pwojè Toupwisan an, mwen p ap kache l.
12 Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
Gade byen, nou tout gen tan wè sa. Ebyen, poukisa nou aji nan foli?
13 “Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
“Sa se pòsyon a moun mechan an ki va sòti Bondye, ak eritaj ke mechan yo va resevwa nan men Toupwisan an.
14 Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
Malgre fis li yo anpil, yo destine pou nepe. Konsa, desandan li yo ap toujou manke pen.
15 Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
Sila ki swiv li yo va antere nan lamò e vèv li yo p ap kriye pou li.
16 Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
Malgre li fè gwo pil ajan an vin tankou se tè e prepare vètman anpil tankou ajil,
17 zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
li kab prepare l, men se moun ladwati yo k ap mete li, se inosan yo k ap divize ajan an.
18 Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
Li te bati kay li tankou papiyon, oswa tankou kay poto gadyen te fè.
19 Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
Li kouche byen rich, men li pa janm vin genyen ankò; li ouvri zye li, men li pa la.
20 Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
Gwo laperèz yo rive pran l tankou yon flèv. Yon move tan vole retire l pandan lannwit.
21 Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
Van lès la pote l ale e li pati. Li fè l vire tounen kite plas li.
22 Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
Paske l ap plonje sou li san epanye, pandan li eseye envite l chape nan men l.
23 Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”
Pèp la va bat men yo sou li. Yo va sifle sou li kon koulèv, pou li kite plas li a.”

< Yobu 27 >