< Yobu 27 >
1 Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Et Job, ajoutant à ce préambule, dit:
2 “Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
Vive le Seigneur qui m'a ainsi jugé, le Tout-Puissant qui a rempli mon âme d'amertume!
3 nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
Aussi longtemps que je conserverai le souffle, que l'esprit divin résidera en moi,
4 pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
Mes lèvres ne laisseront échapper aucune parole déréglée; mon âme ne concevra aucune pensée inique.
5 Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
Dieu me garde jusqu'à la mort de vous croire justes; je ne cesserai pas de protester de mon innocence.
6 Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
Je ne me suis jamais écarté de l'amour de la justice; ma conscience ne me dit pas que j'aie rien fait de mal.
7 “Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
Puissent donc ceux qui me haïssent être renversés comme des impies! puissent ceux qui s'élèvent contre moi périr comme des pervers!
8 Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
Car quelle peut être l'espérance de l'impie dans ses entreprises? S'est- il appuyé sur le Seigneur pour réussir?
9 Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
Dieu exaucerait-il sa prière? Et aux jours de l'adversité
10 Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
Oserait-il s'adresser librement au Seigneur? S'il l'invoquait, serait-il écouté?
11 “Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
Mais je vais vous apprendre ce que tient en sa main le Seigneur, ce que le Tout-Puissant a auprès de lui; je ne dirai rien que de véritable.
12 Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
Et ne le savez-vous pas, vous qui prononcez vainement des choses vaines?
13 “Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
Voici le sort que le Seigneur réserve aux impies; voici la part que le Tout-Puissant fera aux grands de la terre.
14 Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
Si les fils de l'impie sont nombreux, ils périront par l'épée; s'ils arrivent à l'âge d'homme, ils seront des mendiants.
15 Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
Ceux des siens qui lui survivront auront comme lui une mort funeste; nul pour sa veuve n'aura de commisération.
16 Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
S'il a amassé de l'argent comme des monceaux de terre, et de l'or comme des tas d'argile,
17 zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
Les justes se les approprieront; les hommes sincères vivront de ses richesses.
18 Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
Car sa famille aura disparu comme des vermisseaux, comme des toiles d'araignées.
19 Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
Il s'est couché riche et il touchait à sa fin; il a ouvert les yeux et déjà il n'est plus.
20 Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
Les douleurs ont accouru sur lui comme un torrent; la nuit il a été surpris par un tourbillon.
21 Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
Le vent brûlant le saisira et l'enlèvera de sa maison comme la paille qu'à séparée le vanneur.
22 Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
Et il l'accablera sans lui faire grâce, quelque effort qu'il fasse pour échapper à ses atteintes.
23 Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”
Et il frappera à coups redoublés; et, en sifflant il le chassera de la ville qu'il habitait.