< Yobu 27 >
1 Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Job nastavi svoju besjedu i reče:
2 “Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
“Živoga mi Boga što mi pravdu krati i Svesilnog koji dušu mi zagorča:
3 nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
sve dok duha moga bude još u meni, dok mi dah Božji u nosnicama bude,
4 pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
usne moje neće izustiti zloću niti će laž kakva doći na moj jezik.
5 Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
Daleko od mene da vam dadem pravo, nedužnost svoju do zadnjeg daha branim.
6 Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
Pravde svoje ja se držim, ne puštam je; zbog mojih me dana srce korit' neće.
7 “Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
Neka mi dušmana kob opakog snađe, a mog protivnika udes bezbožnikov!
8 Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
Čemu se nadati može kad vapije i kada uzdiže k Bogu dušu svoju?
9 Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
Hoće li čuti Bog njegove krikove kada se na njega obori nevolja?
10 Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
Zar će se radovat' on u Svesilnome, zar će Boga svakog časa zazivati?
11 “Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
Ali Božju ruku ja ću vam pokazat' i neću vam sakrit namjere Svesilnog.
12 Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
Eto, sve ste sami mogli to vidjeti, što se onda u ispraznosti gubite?”
13 “Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
“Ovu sudbu Bog dosuđuje opakom, ovo baštini silnik od Svemogućeg.
14 Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
Ima li sinova mnogo, mač ih čeka, a porod mu neće imat' dosta kruha.
15 Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
Smrt će sahranit' preživjele njegove i udovice ih oplakivat neće.
16 Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
Ako i srebra k'o praha nagomila, ako i nakupi haljina k'o blata,
17 zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
nek' ih skuplja, odjenut će ih pravednik, ljudi će nedužni podijeliti srebro.
18 Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
Od paučine je kuću sagradio, kolibicu kakvu sebi diže čuvar:
19 Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
bogat je legao, al' po posljednji put; kad oči otvori, ničeg više nema.
20 Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
Usred bijela dana strava ga spopada, noću ga oluja zgrabi i odnese.
21 Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
Istočni ga vjetar digne i odvuče, daleko ga baca od njegova mjesta.
22 Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
Bez milosti njime vitla on posvuda, dok mu ovaj kuša umaći iz ruke.
23 Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”
Rukama plješću nad njegovom propašću i zvižde na njega kamo god došao.