< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job respondió:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
“Qué útil has sido para este débil hombre que soy. Qué solidario has sido con el débil.
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Qué buenos consejos le has dado a este ignorante, demostrando que tienes mucha sabiduría.
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
¿Quién te ayudó a decir estas palabras? ¿Quién te ha inspirado a decir tales cosas?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
“Los muertos tiemblan, los que están bajo las aguas.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
El Seol está desnudo ante Dios, Abadón está descubierto. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Extiende el cielo del norte sobre el espacio vacío; cuelga el mundo sobre la nada.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Recoge la lluvia en sus nubes de tormenta que no se rompen bajo el peso.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Él vela su trono; lo cubre con sus nubes.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Sobre la superficie de las aguas puso una frontera; fijó un límite que divide la luz de las tinieblas.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Las columnas del cielo tiemblan; tiemblan de miedo ante su reprimenda.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Calmó el mar con su poder; porque sabía qué hacer aplastó a Rahab.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
El aliento de su voz embelleció los cielos; con su mano atravesó la serpiente que se desliza.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Esto es sólo un poco de todo lo que hace; lo que oímos de él es apenas un susurro, así que quién puede entender su poder atronador?”

< Yobu 26 >