< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Йов а луат кувынтул ши а зис:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
„Кыт де бине штий ту сэ вий ын ажуторул слэбичуний! Кум дай ту ажутор брацулуй фэрэ путере!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Че буне сфатурь дай ту челуй фэрэ причепере! Че белшуг де ынцелепчуне дай ту ла ивялэ!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
Кэтре чине се ындряптэ кувинтеле тале? Ши ал куй дух ворбеште прин тине?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Ынаинтя луй Думнезеу тремурэ умбреле суб апе ши суб локуиторий лор.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
Ынаинтя Луй, Локуинца морцилор есте гоалэ, адынкул н-аре акопериш. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Ел ынтинде мязэноаптя асупра голулуй ши спынзурэ Пэмынтул пе нимик.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Лягэ апеле ын норий Сэй ши норий ну се спарг суб греутатя лор.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Акоперэ фаца скаунулуй Сэу де домние ши Ышь ынтинде норул песте ел.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
А трас о болтэ пе фаца апелор, ка хотар ынтре луминэ ши ынтунерик.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Стылпий черулуй се клатинэ ши се ынспэймынтэ ла аменинцаря Луй.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Прин путеря Луй тулбурэ маря, прин причеперя Луй ый сфэрымэ фурия.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Суфларя Луй ынсенинязэ черул, мына Луй стрэпунӂе шарпеле фугар.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Ши ачестя сунт доар марӂиниле кэилор Сале, ши нумай адиеря лор ушоарэ ажунӂе пынэ ла ной! Дар тунетул лукрэрилор Луй путерниче чине-л ва аузи?”

< Yobu 26 >