< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Porém Job respondeu e disse:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Como ajudaste aquelle que não tinha força? e sustentaste o braço que não tinha vigor?
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Como aconselhaste aquelle que não tinha sabedoria, e plenamente lhe fizeste saber a causa, assim como era?
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
A quem proferiste palavras? e cujo é o espirito que saiu de ti?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Os mortos tremem debaixo das aguas, com os seus moradores d'ellas.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
O inferno está nú perante elle, e não ha coberta para a perdição. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
O norte estende sobre o vazio: a terra pendura sobre o nada.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Prende as aguas nas suas nuvens, todavia a nuvem não se rasga debaixo d'ellas.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Encobre a face do seu throno, e sobre ella estende a sua nuvem.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Assignalou limite sobre a superficie das aguas ao redor d'ellas, até que se acabem a luz e as trevas.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
As columnas do céu tremem, e se espantam da sua ameaça.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Com a sua força fende o mar, e com o seu entendimento abate a sua soberba.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Pelo seu Espirito ornou os céus: a sua mão formou a serpente enroscadiça.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Eis que isto são só as bordas dos seus caminhos; e quão pouco é o que temos ouvido d'elle! Quem pois entenderia o trovão do seu poder?

< Yobu 26 >