< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Respondens autem Iob, dixit:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Cuius adiutor es? numquid imbecillis? et sustentas brachium eius, qui non est fortis?
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Cui dedisti consilium? forsitan illi qui non habet sapientiam, et prudentiam tuam ostendisti plurimam.
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
Quem docere voluisti? nonne eum, qui fecit spiramentum?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Ecce gigantes gemunt sub aquis, et qui habitant cum eis.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
Nudus est infernus coram illo, et nullum est operimentum perditioni. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Qui extendit Aquilonem super vacuum, et appendit terram super nihilum.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Qui ligat aquas in nubibus suis, ut non erumpant pariter deorsum.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Qui tenet vultum solii sui, et expandit super illud nebulam suam.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Terminum circumdedit aquis, usque dum finiantur lux et tenebrae.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Columnae caeli contremiscunt, et pavent ad nutum eius.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
In fortitudine illius repente maria congregata sunt, et prudentia eius percussit superbum.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Spiritus eius ornavit caelos: et obstetricante manu eius, eductus est coluber tortuosus.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Ecce, haec ex parte dicta sunt viarum eius: et cum vix parvam stillam sermonis eius audierimus, quis poterit tonitruum magnitudinis illius intueri?

< Yobu 26 >