< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Felelt Jób és mondta:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Mint gyámolítottad a tehetetlent, segítetted az erőtlennek karját!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Mit tanácsoltál a bölcsességtelennek s valódi tudást bőven ismertettél!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
Kinek adtál tudtul szavakat s kinek szelleme fakadt belőled?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Az árnyak megreszketnek alul a vizeken és lakóikon.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
Meztelen az alvilág ő előtte s takarója az enyészet neki. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Kiterjeszti az Északot az űr fölé, lebegteti a földet a semmiségen;
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
beköti a vizet felhőibe, s nem hasad meg felleg alatta;
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
befogja a trón felszínét, kiterítette reá fellegét.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Határt vont a vizek színén odáig, hol vége van a világosságnak a sötétség mellett.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Az ég oszlopai megrázkódnak s elámulnak dorgálásától.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Erejével felkavarta a tengert s értelmével összezúzta, Ráhábot.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Fuvallata által derültté válik az ég, átszúrta keze a futó kígyót.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Lám, ezek útjainak szélei, mily csekély nesz az, a mit róla hallunk, de hatalmának dörgését ki foghatja föl!

< Yobu 26 >