< Yobu 26 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Hiob antwortete und sprach:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Wie trefflich hast du der Ohnmacht geholfen, den kraftlosen Arm gestützt,
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
wie trefflich den Unverständigen beraten und Weisheit in Fülle geoffenbart!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
Wem hast du deine Reden vorgetragen, und wessen Geist hat aus dir gesprochen?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Die Schatten selbst werden in Beben versetzt unter den Wassern und ihren Bewohnern.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
Nackt liegt die Unterwelt vor ihm, und unverhüllt der Abgrund. (Sheol )
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Er spannt den Norden über dem Leeren aus, läßt die Erde schweben über dem Nichts.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Er bindet die Wasser in seine Wolken ein, ohne daß unter ihnen das Gewölk zerreißt.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Er verhüllt den Anblick seines Throns, indem er sein Gewölk darüber breitet.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Eine Grenze zog er über den Wassern hin, da, wo sich scheiden Licht und Finsternis.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Des Himmels Säulen werden ins Wanken gebracht und entsetzen sich vor seinem Dräun.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Durch seine Macht hat er das Meer erregt und durch seine Einsicht Rahab zerschmettert.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Durch seinen Hauch wird der Himmel heiter, seine Hand durchbohrte den flüchtigen Drachen.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Und das sind nur die Säume seines Waltens - welch' leis Geflüster nur, das wir vernehmen! Doch wer erfaßt die Donnersprache seiner Allgewalt!