< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Alors, répondant, Job dit:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
De qui es-tu l’aide? est-ce d’un homme faible? et soutiens-tu le bras de celui qui n’est pas fort?
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
À qui as-tu donné conseil? sans doute à celui qui n’a pas de sagesse, et tu as montré ta prudence très grande.
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
Qui as-tu voulu enseigner? n’est-ce pas celui qui a créé le souffle de la vie?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Voilà que gémissent sous les eaux les géants et ceux qui habitent avec eux.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
L’enfer est nu devant lui, et l’abîme n’a aucun voile. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
C’est lui qui étend l’aquilon sur le vide, et suspend la terre sur le néant.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
C’est lui qui lie les eaux dans ses nuées, afin qu’elles ne tombent pas toutes ensemble en bas.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
C’est lui qui tient cachée la face de son trône, et qui étend sur lui son nuage.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Il a posé des limites autour des eaux pour les retenir jusqu’à ce que finissent la lumière et les ténèbres.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Les colonnes des cieux frémissent, et elles tremblent à son clin d’œil.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Par sa puissance, soudain les mers se sont rassemblées, et sa prudence a frappé le superbe.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Son esprit a orné les cieux, et, sa main agissant, un serpent tortueux a été produit.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Voilà ce qui a été dit d’une partie de ses voies; et si c’est avec peine que nous avons entendu un petit mot de sa parole, qui pourra contempler l’éclat des tonnerres de sa grandeur?

< Yobu 26 >