< Yobu 26 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job prit la parole et dit:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Comme tu sais bien venir en aide à la faiblesse! Comme tu prêtes secours au bras sans force!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Quels bons conseils tu donnes à celui qui manque d’intelligence! Quelle abondance de sagesse tu fais paraître!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
A qui s’adressent tes paroles? Et qui est-ce qui t’inspire?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Devant Dieu les ombres tremblent Au-dessous des eaux et de leurs habitants;
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
Devant lui le séjour des morts est nu, L’abîme n’a point de voile. (Sheol )
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Il étend le septentrion sur le vide, Il suspend la terre sur le néant.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Il renferme les eaux dans ses nuages, Et les nuages n’éclatent pas sous leur poids.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Il couvre la face de son trône, Il répand sur lui sa nuée.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Il a tracé un cercle à la surface des eaux, Comme limite entre la lumière et les ténèbres.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Les colonnes du ciel s’ébranlent, Et s’étonnent à sa menace.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Par sa force il soulève la mer, Par son intelligence il en brise l’orgueil.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Son souffle donne au ciel la sérénité, Sa main transperce le serpent fuyard.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Ce sont là les bords de ses voies, C’est le bruit léger qui nous en parvient; Mais qui entendra le tonnerre de sa puissance?