< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Et Job répondit et dit:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Comme tu as aidé celui qui n’avait pas de puissance! Comme tu as délivré le bras qui était sans force!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Quel conseil tu as donné à celui qui n’avait pas de sagesse! et quelle abondance d’intelligence tu as montrée!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
Pour qui as-tu prononcé des paroles, et de qui est le souffle qui est sorti de toi?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Les trépassés tremblent au-dessous des eaux et de ceux qui les habitent.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
Le shéol est à nu devant lui, et l’abîme n’a pas de voile. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Il étend le nord sur le vide, il suspend la terre sur le néant.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Il serre les eaux dans ses nuages, et la nuée ne se fend pas sous elles;
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Il couvre la face de son trône et étend ses nuées par-dessus.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Il a tracé un cercle fixe sur la face des eaux, jusqu’à la limite extrême où la lumière confine aux ténèbres.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Les colonnes des cieux branlent et s’étonnent à sa menace.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Il soulève la mer par sa puissance, et, par son intelligence, il brise Rahab.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Par son Esprit le ciel est beau; sa main a formé le serpent fuyard.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Voici, ces choses sont les bords de ses voies, et combien faible est le murmure que nous en avons entendu! Et le tonnerre de sa force, qui peut le comprendre?

< Yobu 26 >