< Yobu 26 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Alors Job répondit,
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
« Comment avez-vous aidé celui qui est sans force! Comment avez-vous sauvé le bras qui n'a pas de force!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Comment avez-vous conseillé celui qui n'a pas de sagesse? et des connaissances solides déclarées en abondance!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
A qui avez-vous adressé des paroles? Quel esprit est sorti de toi?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
« Les esprits défunts tremblent, ceux qui se trouvent sous les eaux et tous ceux qui y vivent.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
Le séjour des morts est nu devant Dieu, et Abaddon n'a pas de couverture. (Sheol )
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Il étend le nord sur l'espace vide, et accroche la terre à rien.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Il enferme les eaux dans ses nuages épais, et le nuage n'est pas éclaté sous eux.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Il entoure la face de son trône, et y répand son nuage.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Il a décrit une frontière à la surface des eaux, et aux confins de la lumière et de l'obscurité.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Les piliers du ciel tremblent et s'étonnent de sa réprimande.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Il remue la mer par sa puissance, et par son intelligence, il frappe à travers Rahab.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
C'est par son Esprit que les cieux sont garnis. Sa main a transpercé le serpent rapide.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Voici, ce ne sont là que les abords de ses voies. Quel faible murmure nous entendons de lui! Mais le tonnerre de sa puissance, qui peut le comprendre? »