< Yobu 26 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Bvt Iob answered, and sayde,
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Whom helpest thou? him that hath no power? sauest thou the arme that hath no strength?
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Whome counsellest thou? him that hath no wisedome? thou shewest right well as the thing is.
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
To whom doest thou declare these words? or whose spirit commeth out of thee?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
The dead things are formed vnder the waters, and neere vnto them.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
The graue is naked before him, and there is no couering for destruction. (Sheol )
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
He stretcheth out the North ouer the emptie place, and hangeth the earth vpon nothing.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
He bindeth the waters in his cloudes, and the cloude is not broken vnder them.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
He holdeth backe the face of his throne: and spreadeth his cloude vpon it.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
He hath set bounds about the waters, vntil the day and night come to an ende.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
The pillars of heauen tremble and quake at his reproofe.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
The sea is calme by his power, and by his vnderstanding he smiteth the pride thereof.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
His Spirite hath garnished the heauens, and his hand hath formed the crooked serpent.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Loe, these are part of his wayes: but how litle a portion heare we of him? and who can vnderstand his fearefull power?