< Yobu 26 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job antwoordde, en sprak
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Hoe goed weet ge den zwakke te helpen, De krachteloze arm te stutten?
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Hoe weet ge den onwetende raad te geven, En wat wijze lessen spreidt ge ten toon?
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
Met wiens hulp hebt ge uw woord gesproken Wiens geest is van u uitgegaan?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
De schimmen beven onder de aarde De wateren sidderen met die erin wonen;
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol )
Het dodenrijk ligt naakt voor zijn oog, De onderwereld zonder bedekking. (Sheol )
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Hij spant het Noorden over de baaierd, Hangt de aarde boven het niet;
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Hij knevelt de wateren in zijn zwerk, De wolken bersten niet onder haar last;
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Hij bedekt het gelaat der volle maan, En spreidt er zijn nevel over uit.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Hij trekt een kring langs de waterspiegel, Waar het licht aan de duisternis grenst;
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
De zuilen van de hemel staan te waggelen, Rillen van angst voor zijn donderende stem.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Hij zwiept de zee door zijn kracht, Ranselt Ráhab door zijn beleid;
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Zijn adem blaast de hemel schoon, Zijn hand doorboort de vluchtende Slang!
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Is dit nog enkel de zoom van zijn wegen Hoe weinig verstaan wij ervan, En wie begrijpt dan de kracht van zijn donder?