< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Da svarede Job og sagde:
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
Hvad har du hjulpet den, som ingen Kraft havde? frelste du den Arm, som ingen Styrke havde?
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
Hvorledes raadede du den, som ingen Visdom havde, og kundgjorde Indsigt til Overflod?
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
For hvem har du kundgjort Tale, og hvis Aande talte ud af dig?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Dødningerne bæve neden under Vandene og deres Beboere.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
Dødsriget ligger blottet for ham, og Afgrunden har intet Skjul. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
Han udbreder Norden over det øde, han hænger Jorden paa intet.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
Han binder Vandet sammen i sine Skyer, dog brister Skydækket ikke under dem.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
Han lukker for sin Trone, han udbreder sin Sky over den.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
Han har draget en Grænse oven over Vandene indtil der, hvor Lyset ender i Mørke.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
Himmelens Piller skælve og forfærdes for hans Trusel.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
Ved sin Kraft oprører han Havet, og med sin Forstand bryder han dets Hovmod.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
Ved hans Aande blive Himlene dejlige; hans Haand gennemborer den flygtende Slange.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Se, disse ere de yderste Grænser af hans Veje, og hvor svag er Lyden af det Ord, som vi have hørt deraf? Men hans Vældes Torden — hvo forstaar den!

< Yobu 26 >