< Yobu 25 >

1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Entonces Bildad el Suhita respondió,
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
“El dominio y el temor están con él. Él hace la paz en sus lugares altos.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
¿Se pueden contar sus ejércitos? ¿Sobre quién no surge su luz?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
¿Cómo puede entonces el hombre ser justo con Dios? ¿O cómo puede estar limpio el que ha nacido de una mujer?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
He aquí que hasta la luna no tiene brillo, y las estrellas no son puras a su vista;
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
Cuánto menos el hombre, que es un gusano, y el hijo del hombre, que es un gusano”.

< Yobu 25 >