< Yobu 25 >

1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Respondens autem Baldad Suhites, dixit:
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
Potestas et terror apud eum est, qui facit concordiam in sublimibus suis.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Numquid est numerus militum eius? et super quem non surget lumen illius?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
Numquid iustificari potest homo comparatus Deo, aut apparere mundus natus de muliere?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
Ecce luna etiam non splendet, et stellae non sunt mundae in conspectu eius:
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
Quanto magis homo putredo, et filius hominis vermis?

< Yobu 25 >