< Yobu 25 >

1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Or, répondant, Baldad, le Subite, dit:
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
La puissance et la terreur sont en celui qui établit la concorde dans ses lieux élevés.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Est-ce qu’on peut compter le nombre de ses soldats? et sur qui sa lumière ne se lèvera-t-elle pas?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
Est-ce qu’un homme peut être justifié, étant comparé à Dieu, ou celui qui est né d’une femme paraître pur?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
Voilà que la lune même ne brille point et que les étoiles ne sont pas pures en sa présence;
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
Combien plus est impur un homme qui est pourriture, un fils de l’homme qui est un ver!

< Yobu 25 >