< Yobu 25 >

1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Forsothe Baldach Suytes answeride, and seide,
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
Power and drede is anentis hym, that is, God, that makith acordyng in hise hiye thingis.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Whether noumbre is of hise knyytis? and on whom schyneth not his liyt?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
Whether a man comparisound to God mai be iustified, ether borun of a womman mai appere cleene?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
Lo! also the moone schyneth not, and sterris ben not cleene in `his siyt;
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
hou miche more a man rot, and the sone of a man a worm, is vncleene `and vile, if he is comparisound to God.

< Yobu 25 >