< Yobu 25 >

1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Then answered Bildad the Shuhite, and said,
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
Dominion and fear are with him; he maketh peace in his high places.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Is there any number of his armies? and upon whom doth not his light arise?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
How then can man be just with God? or how can he be clean that is born of a woman?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
Behold, even the moon hath no brightness, and the stars are not pure in his sight:
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
How much less man, that is a worm! and the son of man, which is a worm!

< Yobu 25 >