< Yobu 25 >

1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Then Bildad the Shuhite spoke up and said,
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
“Dominion and awe belong to God. He brings peace to his heavens.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Who can count his armies? Is there anywhere his light doesn't shine?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
How can a human being be right before God? Can anyone born of woman be pure?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
If in God's eyes even the moon does not shine brightly, and the stars are not pure,
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
how much less a human being—who by comparison is like a maggot or a worm!”

< Yobu 25 >