< Yobu 25 >
1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Then Baldad the Suhite answered, and I said:
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
Power and terror are with him, who maketh peace in his high places.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Is there any numbering of his soldiers? and upon whom shall not his light arise?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
Can man be justified compared with God, or he that is born of a woman appear clean?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
Behold even the moon doth not shine, and the stars are not pure in his sight.
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
How much less man that is rottenness and the son of man who is a worm?