< Yobu 25 >

1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Then Bildad the Shuhite made answer and said,
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
Rule and power are his; he makes peace in his high places.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Is it possible for his armies to be numbered? and on whom is not his light shining?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
How then is it possible for man to be upright before God? or how may he be clean who is a son of woman?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
See, even the moon is not bright, and the stars are not clean in his eyes:
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
How much less man who is an insect, and the son of man who is a worm!

< Yobu 25 >