< Yobu 25 >
1 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Then Bildad the Shuhite replied:
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
“Dominion and awe belong to God; He establishes harmony in the heights of heaven.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
Can His troops be numbered? On whom does His light not rise?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
How then can a man be just before God? How can one born of woman be pure?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
If even the moon does not shine, and the stars are not pure in His sight,
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
how much less man, who is but a maggot, and the son of man, who is but a worm!”