< Yobu 24 >

1 “Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
Для чо́го часи́ не заховані від Всемогу́тнього? Ті ж, що знають Його, Його днів не побачать!
2 Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
Пересо́вують ме́жі безбожні, стадо грабують вони та пасу́ть,
3 Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
займають осла в сироти́ни, беруть у заста́ву вола від удовиць.
4 Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
вони бідних з дороги спиха́ють, разом мусять ховатися збі́джені кра́ю.
5 Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
Тож вони, бідарі́, немов дикі осли на пустині, вихо́дять на працю свою, здобичі шукаючи, — степ йому хліба дає для дітей.
6 Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
На полі вночі вони жнуть, і збирають собі виноград у безбожного,
7 Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
на́го ночують вони, без одежі, і не мають вкриття́ собі в холоді,
8 Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
мокнуть від зливи гірсько́ї, а засло́ни не маючи, скелю вони обіймають.
9 Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
Сироту́ відривають від перс, і в заста́ву беруть від убогого.
10 Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
Ходять на́го вони, без вбрання́, і голодними носять снопи́.
11 Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
Хоч між му́рами їхніми ро́блять оливу, то́пчуть чави́ла, — та прагнуть вони!
12 Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
Стогнуть люди із міста, і кричить душа вби́ваних, а Бог на це зло не зверта́є уваги.
13 “Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
Вони проти світла бунту́ють, не знають дорі́г Його, і на сте́жках Його не сидять.
14 Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
На світа́нку встає душогу́б, замордо́вує бідного та злидаря́, а ніч він прово́дить, як зло́дій.
15 Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
А перелю́бника око чекає смерка́ння, говорячи: „Не побачить мене жодне око!“і засло́ну кладе на обличчя.
16 Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
Підко́пуються під доми́ в темноті́, замика́ються вдень, світла не знають вони,
17 Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
бо ра́нок для них усіх ра́зом — то те́мрява, і знають вони жахи те́мряви.
18 “Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
Такий легкий він на пове́рхні води, на землі їхня частка прокля́та, — не ве́рнеться він на дорогу садів-виноградів.
19 Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol h7585)
Як посу́ха та спе́ка їдять сніжну во́ду, так шео́л поїсть грі́шників! (Sheol h7585)
20 Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
Забуде його лоно матері, буде жерти черва́ його, мов солодо́щі, більше не буде він зга́дуваний, — і безбожник поламаний буде, мов де́рево!
21 Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
Чинить зло для бездітної він, щоб вона не родила, і вдовиці не зробить добра́.
22 Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
А міццю своєю він тягне могутніх, — коли він встає, то ніхто вже не певний свойо́го життя!
23 Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
Бог дає йому все на безпе́ку, і на те він спира́ється, та очі Його бачать їхні доро́ги:
24 Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
піді́ймуться трохи — й не має вже їх, бо понижені. Як усе, вони гинуть, — і зрі́зуються, немов та колоско́ва голо́вка.
25 “Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”
Якщо ж ні, то хто зробить мене неправдомо́вцем, а слово моє на марно́ту обе́рне?“

< Yobu 24 >