< Yobu 24 >

1 “Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
Les temps ne sont pas cachés au Tout-Puissant; mais ceux qui le connaissent ignorent ses jours.
2 Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
Les uns ont transporté des bornes, ravi des troupeaux, et les ont fait paître.
3 Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
Ils ont chassé l’âne des pupilles, et ils ont enlevé pour gage le bœuf de la veuve.
4 Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
Ils ont détruit la voie du pauvre, et ils ont pareillement opprimé les hommes doux de la terre,
5 Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
Les autres, comme les onagres dans le désert, sortent pour leur ouvrage; veillant à leur proie, ils préparent du pain à leurs enfants.
6 Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
Ils moissonnent le champ qui n’est pas à eux; ils vendangent la vigne de celui qu’ils ont opprimé par la force.
7 Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
Ils renvoient des hommes tout nus, enlevant les vêtements à ceux qui n’ont pas de quoi se couvrir pendant le froid,
8 Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
Que les pluies des montagnes inondent, et qui n’ayant pas de vêtement, se réfugient dans des rochers.
9 Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
Ils ont usé de violence, pillant des orphelins; et le pauvre peuple, ils l’ont dépouillé.
10 Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
À ceux qui étaient nus et qui allaient sans vêtements, et à ceux qui avaient faim, ils ont pris des épis.
11 Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
Ils ont fait la méridienne au milieu des tas de fruits de ceux qui, après avoir foulé des pressoirs, avaient soif.
12 Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
Dans les villes, ils ont fait gémir les hommes, et l’âme des blessés a crié, et Dieu ne souffre pas que ce mal passe impuni.
13 “Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
Ils ont été rebelles à la lumière; ils n’ont pas connu les voies de Dieu, et ils ne sont pas revenus par ses sentiers,
14 Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
L’homicide se lève dès le grand matin, il tue l’indigent et le pauvre; et pendant la nuit, il sera comme un voleur.
15 Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
L’œil d’un adultère épie l’obscurité, disant: Aucun œil ne me verra; et il couvrira son visage.
16 Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
Il perce des maisons dans les ténèbres, comme ils en étaient convenus pendant le jour; et ils n’ont pas connu la lumière.
17 Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
Si tout d’un coup apparaît l’aurore, ils croient que c’est l’ombre de la mort; et ainsi dans les ténèbres, ils marchent comme à la lumière.
18 “Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
Il est plus léger que la face de l’eau; maudite soit sa part sur la terre, et qu’il ne marche point par le chemin des vignes.
19 Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol h7585)
Qu’il passe des eaux des neiges à une excessive chaleur, et que jusques aux enfers son péché le conduise. (Sheol h7585)
20 Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
Que la miséricorde l’oublie; que les vers soient ses délices; qu’il ne soit point dans le souvenir des hommes; mais qu’il soit brisé comme un arbre infructueux.
21 Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
Car il a nourri la femme stérile, qui n’enfante pas, et il n’a pas fait de bien à la veuve.
22 Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
il a abattu des hommes forts par sa puissance; et lorsqu’il sera ferme, il ne croira pas en sa vie.
23 Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
Dieu lui a donné lieu de faire pénitence, et lui en abuse pour s’enorgueillir; mais les yeux de Dieu sont sur ses voies.
24 Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
Ils se sont élevés pour un moment, et ils ne subsisteront pas; ils seront humiliés comme toutes choses, puis ils seront emportés, et brisés comme des sommités d’épis.
25 “Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”
Que s’il n’en est pas ainsi, qui peut me convaincre d’avoir menti, et mettre devant Dieu mes paroles?

< Yobu 24 >