< Yobu 24 >
1 “Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
The times are not hidden from the Almighty; even those who know him, do not know his days.
2 Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
Some have crossed the boundaries, plundered the flocks, and given them pasture.
3 Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
They have driven away the donkey of orphans, and have taken the cow from the widow as collateral.
4 Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
They have undermined the way of the poor, and have pressed together the meek of the earth.
5 Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
Others, like wild asses in the desert, go forth to their work; by watching for prey, they obtain bread for their children.
6 Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
They reap a field that is not their own, and they harvest a vineyard that they have taken by force.
7 Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
They send men away naked, having taken the clothing of those who have no covering in the cold;
8 Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
these are wet with the mountain rain, and, having no covering, they embrace the rocks.
9 Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
They have used violence to deprive orphans, and they have robbed the poor common people.
10 Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
From the naked and those who do not have enough clothing, and from the hungry, they have taken away sheaves of grain.
11 Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
They take their midday rest among the stockpiles of those who, though they have trodden the winepresses, suffer thirst.
12 Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
In the cities, they caused the men to groan and the spirit of the wounded to cry out, and so God does not allow this to go unpunished.
13 “Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
They have been rebellious against the light; they have not known his ways, nor have they returned by his paths.
14 Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
The killer of men rises at first light; he executes the destitute and the poor, but, in truth, he is like a thief in the night.
15 Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
The eye of the adulterer waits for darkness, saying, “No eye will see me,” and he covers his face.
16 Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
He passes through houses in the nighttime, just as they had agreed among themselves in the daytime; and they are ignorant of the light.
17 Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
If sunrise should suddenly appear, it is treated by them like the shadow of death; and they walk in darkness, as if in light.
18 “Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
He is nimble on the surface of water. His place on land is to be accursed. May he not walk by way of the vineyards.
19 Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol )
May he cross from the snowy waters to excessive heat, and his sin, all the way to hell. (Sheol )
20 Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
Let mercy forget him. His charm is worms. Let him not be remembered, but instead be broken like an unfruitful tree.
21 Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
For he has fed on the barren, who does not bear fruit, and he has not done good to the widow.
22 Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
He has pulled down the strong by his strength, and, when he stands up, he will not have trust in his life.
23 Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
God has given him a place for repentance, and he abuses it with arrogance, but his eyes are upon his ways.
24 Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
They are lifted up for a little while, but they will not continue, and they will be brought low, just like all things, and they will be taken away, and, like the tops of the ears of grain, they will be crushed.
25 “Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”
But, if this is not so, who is able to prove to me that I have lied and to place my words before God?