< Yobu 23 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
А Йов відповів та й сказав:
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
„Моя мова й сьогодні гірка́, — тяжче стражда́ння моє за стогна́ння мої.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
О, якби то я знав, де Його я знайду́, то прийшов би до місця Його пробува́ння!
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
Я б перед обличчям Його свою справу поклав, а уста свої я напо́внив би до́водами, —
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
розізнав би слова́, що́ мені відповість, і я зрозумів би, що́ скаже мені.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
Чи зо мною на прю Він з великою силою стане? О ні, — тільки б увагу звернув Він на мене!
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
Справедливий судився б там з Ним, я ж наза́вжди б звільни́всь від свойого Судді.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Та піду́ я на схід — і немає Його, а на за́хід удамся — Його не побачу,
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
на півно́чі шукаю Його — й не вхоплю́, збо́чу на пі́вдень — і не добача́ю.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
А Він знає дорогу, яка при мені, — хай би ви́пробував Він мене, — мов те золото, вийду!
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
Трималась нога моя коло стопи́ Його, доро́ги Його я держа́вся й не збо́чив.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
Я не відступався від за́повідей Його губ, над уста́ву свою я ховав слова уст Його.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
Але Він при одно́му, — й хто заве́рне Його? Як чого зажадає душа Його, — те Він учинить:
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
бо Він ви́конає, що́ про мене призна́чив, і в Нього багато такого, як це!
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Тому перед обличчям Його я тремчу́, розважаю — й жахаюсь Його.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
А Бог пом'якши́в моє серце, і Всемогутній мене настраши́в,
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
бо не знищений я від темно́ти, ані від обличчя свого, що темність закрила його!

< Yobu 23 >