< Yobu 23 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job respondió:
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
Aun hoy es amarga mi queja, pues mi llaga agrava mis gemidos.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
¡Ojalá me concediera saber dónde hallarlo! Yo iría hasta su trono,
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
expondría ante Él mi causa, llenaría mi boca de argumentos,
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
sabría con cuáles palabras me replica, y entendería lo que me dice.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
¿Contendería conmigo con la grandeza de su fuerza? No, más bien me atendería.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
Allí el justo podría razonar con Él, y yo quedaría libre para siempre de mi Juez.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Pero si voy hacia el oriente, no está allí. Y si voy al occidente, tampoco lo percibo.
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
Si muestra su poder en el norte, no lo veré, al sur se esconde y no lo veo.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
Sin embargo, Él conoce el camino por donde voy. Que me pruebe, y saldré como oro.
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
Mis pies siguieron fielmente sus huellas. Guardé su camino sin apartarme.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
No retrocedí del mandato de sus labios, y atesoré las Palabras de su boca más que mi ración necesaria.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
Pero Él es único. ¿Quién podrá disuadirlo? Él hace lo que desea.
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
Él ejecutará lo que decretó para mí, y muchas otras cosas como ésta están en Él.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Por lo cual me perturba su Presencia. Al pensarlo, me aterrorizo de Él.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
Porque ʼElohim hizo desmayar mi corazón. ʼEL-Shadday me aterrorizó.
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
Pues no fui cortado de la presencia de la tenebrosidad, y Él no escondió mi semblante de la profunda oscuridad.