< Yobu 23 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
A odpowiadając Ijob rzekł:
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
Czemuż jeszcze uporem zowiecie narzekanie moje, choć bieda moja cięższa jest niż wzdychanie moje?
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
Obym wiedział, gdziebym go mógł znaleść, szedłbym aż do stolicy jego.
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
Przełożyłbym przed nim sprawę moję, a usta moje napełniłbym dowodami.
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
Dowiedziałbym się, jakoby mi odpowiedział, a zrozumiałbym, coby mi rzekł.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
Izaż się w wielkości siły swojej będzie spierał ze mną? Nie; i owszem sam mi doda siły.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
Tamby się człowiek szczery rozprawił z nim, i byłbym wolnym wiecznie od sędziego mego.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Ale oto, pójdęli wprost, niemasz go; a jeźli nazad, nie dojdę go.
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
Pójdęli w lewo, choćby zatrudniony był, nie oglądam go; ukryłliby się w prawo, nie ujrzę go,
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
Gdyż on zna drogę moję; a będzieli mię doświadczał, jako złoto wynijdę.
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
Śladu jego trzymała się noga moja; drogim jego przestrzegał, a nie zstępowałem z niej.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
Od przykazania ust jego nie odchylałem się; owszem, postanowiłem u siebie zachować słowa ust jego.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
Jeźli on przy swem stanie, któż go odwróci? bo co dusza jego żąda, to uczyni:
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
Bo on wykona, co postanowił o mnie, a takowych przykładów dosyć jest u niego.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Przetoż od oblicza jego strwożyłem się, a uważając to, lękam się go.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
Bóg zemdlił serce moje, a Wszechmocny zatrwożył mną.
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
Tak, żem mało nie zginął od ciemności; bo przed oblicznością moją nie zakrył zamroczenia.