< Yobu 23 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Waphendula uJobe wathi:
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
“Lalamuhla ukusola kwami kulokhu kubuhlungu kabi, isandla sakhe siyasinda loba ngibubula kangaka.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
Ngabe ngiyakwazi lapho engingamfumana khona; aluba nje bengingaya emzini wakhe!
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
Bengizayibeka kuhle indaba yami phambi kwakhe ngigcwalise umlomo wami ngamazwi empikiswano.
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
Bengizakuzwa ukuthi yena uphendula athini, ngikuhlolisise lokho akutshoyo.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
Kambe angangiphikisa ngamandla na? Hatshi, angazake angethese cala.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
Lapho umuntu oqotho ubengendlala indaba yakhe phambi kwakhe, njalo bengizakhululwa lanini kumahluleli wami.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Kodwa nxa ngisiya empumalanga, yena kakho khona; nxa ngisiya entshonalanga, kangimfumani khona.
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
Nxa esemsebenzini enyakatho, kangimboni; angaphendukela eningizimu, kangiboni lokuthi tshazi kwakhe.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
Kodwa uyayazi indlela engihamba ngayo; nxa esengilingile, ngizaphuma senginjengegolide.
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
Inyawo zami bezilokhu zilandelana lezinyathelo zakhe; ngalela endleleni yakhe angaze ngaphambuka.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
Angigudlukanga emilayweni yezindebe zakhe; ngiwenze igugu amazwi omlomo wakhe ukwedlula isinkwa sami sansukuzonke.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
Kodwa uzimele yedwa, ngubani ongaphikisana laye na? Uyenza loba yini ayifunayo.
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
Uyagcwalisa isimiso sakhe ngami, njalo manengi amacebo anjalo awagcinileyo.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Yikho-nje ngithuthumela ukuma phambi kwakhe; ngithi ngingakukhumbula konke lokhu ngimesabe.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
UNkulunkulu usenze inhliziyo yami yaphela amandla; uSomandla usengethusile.
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
Kodwa kawuyikungithulisa umnyama lo, umnyama lo onzima ovala ubuso bami.”

< Yobu 23 >