< Yobu 23 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Hoe ty natoi’ Iobe:
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
Mafaitse ty toreoko henaneo, taña-miletraletra ty amy hatreontreoko.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
Ehe te napotako ty hahatreavako Aze, hiheovako mb’am-piambesa’e mb’eo.
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
Halahako aolo’e eo ty amako, vaho hatsafeko veroke ty vavako.
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
Ho azoko ty entañe havale’e ahy, vaho ho rendreko ty hitsara’e.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
Hatreatré’e ami’ty hara’elahin-kaozara’e hao? Aiy, f’ie ho haoñe’e.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
Mete hilahatse ama’e ty vañoñe, hamotsorañe ahy nainai’e amy Mpizakakoy.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Hehe te mionjon-draho, f’ie tsy eo, midisa-voly, fa tsy isako,
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
ie mitoloñ’an-kavia, tsy treako, ie mitolike mb’àn-kavana, tsy rendreko.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
Fe arofoana’e ty lala fombàko, ie fa nitsoeha’e le hiboake hoe volamena.
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
Nahafitinoñe i lia’ey ty tomboko, nifaharako i lala’ey vaho tsy nitsile.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
Tsy nisitahako o nafèm-pivimbi’eo; nahajako o tsaram-palie’eo mandikoatse ty anjara rimako.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
F’ie tsy roe tsy telo, ia ty hampitolik’ aze? anoe’e iaby ze satrin’arofo’e.
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
Ie ro mañeneke o atolots’ ahikoo: maro ty fanoe’e hoe Izay.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Aa le hirevendreven-draho añ’atrefa’e eo; izaho mitsakore, le añeveñako.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
Ampianifan’ Añahare ty troko, ampangebahebae’ i El-Sadai,
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
Toe tsy naitoañ’ añatrefa’ i ieñey iraho, naho nisaroña’e an-tareheko i fimoromoroñañey.

< Yobu 23 >