< Yobu 23 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Respondens autem Iob, ait:
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
Nunc quoque in amaritudine est sermo meus, et manus plagæ meæ aggravata est super gemitum meum.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
Quis mihi tribuat ut cognoscam et inveniam illum, et veniam usque ad solium eius?
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
Ponam coram eo iudicium, et os meum replebo increpationibus.
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
Ut sciam verba, quæ mihi respondeat, et intelligam quid loquatur mihi.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
Nolo multa fortitudine contendat mecum, nec magnitudinis suæ mole me premat.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
Proponat æquitatem contra me, et perveniat ad victoriam iudicium meum.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Si ad Orientem iero, non apparet: si ad Occidentem, non intelligam eum.
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
Si ad sinistram, quid agam? non apprehendam eum: si me vertam ad dexteram, non videbo illum.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
Ipse vero scit viam meam, et probavit me quasi aurum, quod per ignem transit:
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
Vestigia eius secutus est pes meus, viam eius custodivi, et non declinavi ex ea.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
A mandatis labiorum eius non recessi, et in sinu meo abscondi verba oris eius.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
Ipse enim solus est, et nemo avertere potest cogitationem eius: et anima eius quodcumque voluit, hoc fecit.
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
Cum expleverit in me voluntatem suam, et alia multa similia præsto sunt ei.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Et idcirco a facie eius turbatus sum, et considerans eum, timore sollicitor.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
Deus mollivit cor meum, et Omnipotens conturbavit me.
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
Non enim perii propter imminentes tenebras, nec faciem meam operuit caligo.

< Yobu 23 >