< Yobu 23 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
ויען איוב ויאמר
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
גם-היום מרי שחי ידי כבדה על-אנחתי
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
מי-יתן ידעתי ואמצאהו אבוא עד-תכונתו
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
אערכה לפניו משפט ופי אמלא תוכחות
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
אדעה מלים יענני ואבינה מה-יאמר לי
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
הברב-כח יריב עמדי לא אך-הוא ישם בי
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
שם--ישר נוכח עמו ואפלטה לנצח משפטי
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
הן קדם אהלך ואיננו ואחור ולא-אבין לו
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
שמאול בעשתו ולא-אחז יעטף ימין ולא אראה
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
כי-ידע דרך עמדי בחנני כזהב אצא
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
באשרו אחזה רגלי דרכו שמרתי ולא-אט
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
מצות שפתיו ולא אמיש מחקי צפנתי אמרי-פיו
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
והוא באחד ומי ישיבנו ונפשו אותה ויעש
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
כי ישלים חקי וכהנה רבות עמו
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
על-כן מפניו אבהל אתבונן ואפחד ממנו
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
ואל הרך לבי ושדי הבהילני
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
כי-לא נצמתי מפני-חשך ומפני כסה-אפל

< Yobu 23 >