< Yobu 23 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
And Job answereth and saith: —
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
Also — to-day [is] my complaint bitter, My hand hath been heavy because of my sighing.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
O that I had known — and I find Him, I come in unto His seat,
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
I arrange before Him the cause, And my mouth fill [with] arguments.
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
I know the words He doth answer me, And understand what He saith to me.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
In the abundance of power doth He strive with me? No! surely He putteth [it] in me.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
There the upright doth reason with Him, And I escape for ever from my judge.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Lo, forward I go — and He is not, And backward — and I perceive him not.
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
[To] the left in His working — and I see not, He is covered [on] the right, and I behold not.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
For He hath known the way with me, He hath tried me — as gold I go forth.
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
On His step hath my foot laid hold, His way I have kept, and turn not aside,
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
The command of His lips, and I depart not. Above my allotted portion I have laid up The sayings of His mouth.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
And He [is] in one [mind], And who doth turn Him back? And His soul hath desired — and He doth [it].
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
For He doth complete my portion, And many such things [are] with Him.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Therefore, from His presence I am troubled, I consider, and am afraid of Him.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
And God hath made my heart soft, And the Mighty hath troubled me.
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
For I have not been cut off before darkness, And before me He covered thick darkness.