< Yobu 23 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Sotheli Joob answeride, and seide,
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
Now also my word is in bitternesse, and the hond of my wounde is agreggid on my weilyng.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
Who yyueth to me, that Y knowe, and fynde hym, and come `til to his trone?
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
Y schal sette doom bifor hym, and Y schal fille my mouth with blamyngis;
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
that Y kunne the wordis, whiche he schal answere to me, and that Y vnderstonde, what he schal speke to me.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
Y nyle, that he stryue with me bi greet strengthe, nether oppresse me with the heuynesse of his greetnesse.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
Sette he forth equite ayens me, and my doom come perfitli to victorie.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
If Y go to the eest, God apperith not; if Y go to the west, Y schal not vndurstonde hym; if Y go to the left side,
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
what schal Y do? Y schal not take hym; if Y turne me to the riyt side, Y schal not se hym.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
But he knowith my weie, and he schal preue me as gold, that passith thorouy fier.
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
My foot suede hise steppis; Y kepte his weie, and Y bowide not awey fro it.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
Y yede not awei fro the comaundementis of hise lippis; and Y hidde in my bosum the wordis of his mouth.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
For he is aloone, and no man may turne awei hise thouytis; and what euer thing he wolde, his wille dide this thing.
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
Whanne he hath fillid his wille in me, also many othere lijk thingis ben redi to hym.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
And therfor Y am disturblid of his face, and Y biholdynge hym am anguyschid for drede.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
God hath maad neische myn herte, and Almyyti God hath disturblid me.
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
For Y perischide not for derknessis neiyynge; nethir myist hilide my face.