< Yobu 23 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
And Job answered and said,
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
Even to-day is my complaint bitter: my stroke is heavier than my groaning.
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
Oh that I knew where I might find him, that I might come to his seat!
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
I would order the cause before him, and fill my mouth with arguments;
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
I would know the words he would answer me, and understand what he would say unto me.
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
Would he plead against me with [his] great power? Nay; but he would give heed unto me.
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
There would an upright man reason with him; and I should be delivered for ever from my judge.
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
Lo, I go forward, but he is not there; and backward, but I do not perceive him;
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
On the left hand, where he doth work, but I behold [him] not; he hideth himself on the right hand, and I see [him] not.
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
But he knoweth the way that I take; he trieth me, I shall come forth as gold.
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
My foot hath held to his steps; his way have I kept, and not turned aside.
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
Neither have I gone back from the commandment of his lips; I have laid up the words of his mouth more than the purpose of my own heart.
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
But he is in one [mind], and who can turn him? And what his soul desireth, that will he do.
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
For he will perform [what] is appointed for me; and many such things are with him.
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
Therefore am I troubled at his presence; I consider, and I am afraid of him.
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
For God hath made my heart soft, and the Almighty troubleth me;
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
Because I was not cut off before the darkness, neither hath he hidden the gloom from me.

< Yobu 23 >