< Yobu 23 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
約伯回答說:
2 “Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
如今我的哀告還算為悖逆; 我的責罰比我的唉哼還重。
3 Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
惟願我能知道在哪裏可以尋見上帝, 能到他的臺前,
4 Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
我就在他面前將我的案件陳明, 滿口辯白。
5 Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
我必知道他回答我的言語, 明白他向我所說的話。
6 Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
他豈用大能與我爭辯嗎? 必不這樣!他必理會我。
7 Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
在他那裏正直人可以與他辯論; 這樣,我必永遠脫離那審判我的。
8 “Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
只是,我往前行,他不在那裏, 往後退,也不能見他。
9 Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
他在左邊行事,我卻不能看見, 在右邊隱藏,我也不能見他。
10 Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
然而他知道我所行的路; 他試煉我之後,我必如精金。
11 Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
我腳追隨他的步履; 我謹守他的道,並不偏離。
12 Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
他嘴唇的命令,我未曾背棄; 我看重他口中的言語,過於我需用的飲食。
13 “Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
只是他心志已定,誰能使他轉意呢? 他心裏所願的,就行出來。
14 Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
他向我所定的,就必做成; 這類的事他還有許多。
15 Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
所以我在他面前驚惶; 我思念這事便懼怕他。
16 Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
上帝使我喪膽; 全能者使我驚惶。
17 Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.
我的恐懼不是因為黑暗, 也不是因為幽暗蒙蔽我的臉。