< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
І заговорив теманянин Еліфа́з та й сказав:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
„Чи для Бога люди́на кори́сна? Бо мудрий кори́сний самому собі!
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Хіба Всемогу́тній бажає, щоб ти ніби праведним був? І що за ко́ристь Йому, як дороги свої ти вважаєш невинними сам?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Чи Він буде карати, тебе боячи́сь, і чи пі́де з тобою на суд?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Хіба твоє зло не велике? Таж твоїм беззако́нням немає кінця!
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Таж з братів своїх брав ти заста́ву даремно, а з наго́го одежу стягав!
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Не поїв ти водою знемо́женого, і від голодного стримував хліб.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
А си́льна люди́на — то їй оцей край, і поче́сний у ньому сидітиме.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Ти напо́рожньо вдів відсилав, і сирі́тські раме́на гноби́лись, —
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
тому па́стки тебе оточи́ли, і жахає тебе наглий страх,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
твоє світло стемні́ло, нічого не бачиш, і велика вода закриває тебе.
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Чи ж Бог не високий, як небо? Та на зо́рі уго́ру поглянь, які стали високі вони!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
А ти кажеш: „Що ві́дає Бог? Чи судитиме Він через млу?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Хмари — завіса Йому, й Він не бачить, і ходить по кру́зі небесному“.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Чи ти будеш триматись дороги відвічної, що нею ступа́ли безбожні,
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
що невча́сно були вони згу́блені, що річка розлита, підвалина їх,
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
що до Бога казали вони: „Відступися від нас!“та: „Що́ зробить для нас Всемогутній?“
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
А Він доми їхні напо́внив добром! Але віддалилась від мене порада безбожних!
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Справедливі це бачать та ті́шаться, і насміхається з нього невинний:
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
„Справді ви́гублений наш противник, а останок їх ви́жер огонь!“
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Заприязни́ся із Ним, та й май спо́кій, — цим при́йде на тебе добро́.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Зако́на візьми з Його уст, а слова Його в серце своє поклади.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Якщо ве́рнешся до Всемогутнього, — будеш збудо́ваний, і віддали́ш беззаконня з наметів своїх.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
І викинь до по́роху золото, і мов камінь з потоку офі́рське те золото, —
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
і буде тобі Всемогу́тній за золото та за срі́бло блискуче тобі!
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Бо тоді Всемогутнього ти покохаєш і до Бога піді́ймеш обличчя своє, —
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
будеш благати Його — й Він почує тебе, і ти обітниці свої надолу́жиш.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
А що́ постано́виш, то ви́повниться те тобі, й на дорогах твоїх буде ся́яти світло.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Бо знижує Він спину пи́шного, хто ж смиренний, тому помагає.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
Рятує Він і небезви́нного, і той чистото́ю твоїх рук урято́ваний буде“.

< Yobu 22 >