< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
پس الیفاز تیمانی در جواب گفت:۱
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
«آیا مرد به خدا فایده برساند؟ البته مرد دانا برای خویشتن مفید است.۲
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
آیا اگر توعادل باشی، برای قادر مطلق خوشی رخ می‌نماید؟ یا اگر طریق خود را راست سازی، او رافایده می‌شود؟۳
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
آیا به‌سبب ترس تو، تو را توبیخ می‌نماید؟ یا با تو به محاکمه داخل خواهد شد؟۴
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
آیا شرارت تو عظیم نیست و عصیان تو بی‌انتهانی،۵
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
چونکه از برادران خود بی‌سبب گرو گرفتی و لباس برهنگان را کندی،۶
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
به تشنگان آب ننوشانیدی، و از گرسنگان نان دریغ داشتی؟۷
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
امامرد جبار، زمین از آن او می‌باشد و مرد عالیجاه، در آن ساکن می‌شود.۸
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
بیوه‌زنان را تهی‌دست رد نمودی، و بازوهای یتیمان شکسته گردید.۹
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
بنابراین دامها تو را احاطه می‌نماید و ترس، ناگهان تو را مضطرب می‌سازد.۱۰
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
یا تاریکی که آن را نمی بینی و سیلابها تو را می‌پوشاند.۱۱
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
آیاخدا مثل آسمانها بلند نیست؟ و سر ستارگان رابنگر چگونه عالی هستند.۱۲
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
و تو می‌گویی خداچه می‌داند و آیا از تاریکی غلیظ داوری تواندنمود؟۱۳
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
ابرها ستر اوست پس نمی بیند، و بردایره افلاک می‌خرامد.۱۴
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
آیا طریق قدما را نشان کردی که مردمان شریر در آن سلوک نمودند،۱۵
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
که قبل از زمان خود ربوده شدند، و اساس آنهامثل نهر ریخته شد۱۶
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
که به خدا گفتند: از ما دورشو و قادر مطلق برای ما چه تواند کرد؟۱۷
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
و حال آنگاه او خانه های ایشان را از چیزهای نیکو پرساخت. پس مشورت شریران از من دور شود.۱۸
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
«عادلان چون آن را بینند، شادی خواهندنمود و بی‌گناهان بر ایشان استهزا خواهند کرد.۱۹
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
آیا مقاومت کنندگان ما منقطع نشدند؟ و آتش بقیه ایشان را نسوزانید؟۲۰
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
پس حال با او انس بگیر و سالم باش. و به این منوال نیکویی به توخواهد رسید.۲۱
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
تعلیم را از دهانش قبول نما، وکلمات او را در دل خود بنه.۲۲
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
اگر به قادرمطلق بازگشت نمایی، بنا خواهی شد. و اگر شرارت رااز خیمه خود دور نمایی۲۳
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
و اگر گنج خود را درخاک و طلای اوفیر را در سنگهای نهرهابگذاری،۲۴
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
آنگاه قادر مطلق گنج تو و نقره خالص برای تو خواهد بود،۲۵
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
زیرا در آنوقت ازقادر مطلق تلذذ خواهی یافت، و روی خود را به طرف خدا برخواهی افراشت.۲۶
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
نزد او دعاخواهی کرد و او تو را اجابت خواهد نمود، و نذرهای خود را ادا خواهی ساخت.۲۷
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
امری راجزم خواهی نمود و برایت برقرار خواهد شد، وروشنایی بر راههایت خواهد تابید.۲۸
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
وقتی که ذلیل شوند، خواهی گفت: رفعت باشد، و فروتنان را نجات خواهد داد.۲۹
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
کسی را که بی‌گناه نباشدخواهد رهانید، و به پاکی دستهای تو رهانیده خواهد شد.»۳۰

< Yobu 22 >