< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Wasephendula uElifazi umThemani wathi:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Umuntu angaba losizo kuNkulunkulu yini, ngoba ohlakaniphileyo elusizo kuye ngokwakhe?
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Kuyintokozo yini kuSomandla ukuthi ulungile? Kumbe inzuzo kuye ukuthi uphelelise indlela zakho?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Uzakusola yini ngenxa yokwesaba kwakho? Uzangena lawe kusahlulelo.
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Ububi bakho kabubukhulu yini, lezono zakho kazilakuphela?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Ngoba uthethe isibambiso kubafowenu kungelasizatho, wahlubula abanqunu izigqoko.
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Kawumnathisanga amanzi odiniweyo, lolambileyo umgodlele ukudla.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Kodwa umuntu olengalo, umhlaba ungowakhe, lowemukeleka ebusweni wahlala kuwo.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Uxotshile abafelokazi bengelalutho, lengalo zezintandane zichotshoziwe.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
Ngakho-ke imijibila ikuhanqile, lovalo luhle lwakwesabisa,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
kumbe ubumnyama ukuze ungaboni, lesikhukhula samanzi sikusibekele.
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
UNkulunkulu kakho yini engqongeni yamazulu? Bona-ke ingqonga yezinkanyezi, ukuthi ziphakeme kangakanani.
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Kanti uthi: UNkulunkulu wazini? Angahlulela yini engemuva komnyama onzima?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Amayezi amnyama ayisisibekelo sakhe ukuze angaboni, uhamba esigombolozini samazulu.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Usunanzelele indlela endala yini abantu ababi abanyathela kuyo?
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
Abahluthunwa kungakabi yisikhathi; uzamcolo wathululwa phezu kwesisekelo sabo.
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
Abathi kuNkulunkulu: Suka kithi. LoSomandla wayenzeni kubo?
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Kanti yena wayegcwalise izindlu zabo ngokuhle; kodwa icebo labakhohlakeleyo likhatshana lami.
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Abalungileyo bayakubona bathokoze, lomsulwa ubahleka usulu.
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
Isibili isitha sethu sichithiwe, lomlilo uqede insali yabo.
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Ake wejwayelane laye, ube lokuthula, ngalokho okuhle kuzakuza kuwe.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Ake wemukele umlayo ovela emlonyeni wakhe, ubeke amazwi akhe enhliziyweni yakho.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Uba ubuyela kuSomandla, uzakwakhiwa, ususe okubi khatshana lamathente akho.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Ubusubeka igolide lakho othulini, legolide leOfiri elitsheni lezifula.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
Ngakho uSomandla uzakuba ligolide lakho, lesiliva sakho esinengi.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Ngoba ngalesosikhathi uzazithokozisa ngoSomandla, uphakamisele ubuso bakho kuNkulunkulu.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Uzakhuleka kuye, akuzwe, ukhokhe izifungo zakho.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Uzaquma-ke udaba, luqiniseke kuwe, lokukhanya kukhanye endleleni zakho.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Nxa behliselwe phansi, ubususithi: Phezulu! Abesesindisa othobekileyo ngamehlo.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
Uzamkhulula ongemsulwa; njalo ukhululwa ngokuhlanzeka kwezandla zakho.

< Yobu 22 >