< Yobu 22 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
是においてテマン人エリパズこたへて曰く
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
人神を益する事をえんや 智人も唯みづから益する而已なるぞかし
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
なんぢ義かるとも全能者に何の歡喜かあらん なんぢ行爲を全たふするとも彼に何の利益かあらん
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
彼汝の畏懼の故によりて汝を責め汝を鞫きたまはんや
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
なんぢの惡大なるにあらずや 汝の罪はきはまり無し
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
即はち汝は故なくその兄弟の物を抑へて質となし 裸なる者の衣服を剥て取り
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
渇く者に水を與へて飮しめず 饑る者に食物を施こさず
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
力ある者土地を得 貴き者その中に住む
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
なんぢは寡婦に手を空しうして去しむ 孤子の腕は折る
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
是をもて網羅なんぢを環り 畏懼にはかに汝を擾す
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
なんぢ黑暗を見ずや 洪水のなんぢを覆ふを見ずや
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
神は天の高に在すならずや 星辰の巓ああ如何に高きぞや
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
是によりて汝は言ふ 神なにをか知しめさん 豈よく黑雲の中より審判するを得たまはんや
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
濃雲かれを蔽へば彼は見たまふ所なし 唯天の蒼穹を歩みたまふ
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
なんぢ古昔の世の道を行なはんとするや 是あしき人の踐たりし者ならずや
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
彼等は時いまだ至らざるに打絶れ その根基は大水に押流されたり
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
彼ら神に言けらく我儕を離れたまへ 全能者われらのために何を爲ことを得んと
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
しかるに彼は却つて佳物を彼らの家に盈したまへり 但し惡人の計畫は我に與する所にあらず
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
義しき者は之を見て喜び 無辜者は彼らを笑ふ
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
曰く我らの仇は誠に滅ぼされ 其盈餘れる物は火にて焚つくさる
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
請ふ汝神と和らぎて平安を得よ 然らば福祿なんぢに來らん
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
請ふかれの口より敎晦を受け その言語をなんぢの心に藏めよ
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
なんぢもし全能者に歸向り且なんぢの家より惡を除き去ば 汝の身再び興されん
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
なんぢの寳を土の上に置き オフルの黄金を谿河の石の中に置け
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
然れば全能者なんぢの寳となり汝のために白銀となりたまふべし
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
而してなんぢは又全能者を喜び且神にむかひて面をあげん
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
なんぢ彼に祈らば彼なんぢに聽たまはん 而して汝その誓願をつくのひ果さん
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
なんぢ事を爲んと定めなばその事なんぢに成ん 汝の道には光照ん
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
其卑く降る時は汝いふ昇る哉と 彼は謙遜者を拯ひたまふべし
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
かれは罪なきに非ざる者をも拯ひたまはん 汝の手の潔淨によりて斯る者も拯はるべし