< Yobu 22 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Da antwortete Eliphas von Theman und sprach:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Was darf Gott eines Starken, und was nützt ihm ein Kluger?
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Meinest du, daß dem Allmächtigen gefalle, daß du dich so fromm machest? Oder was hilft's ihm, ob du deine Wege gleich ohne Wandel achtest?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Meinest du, er wird sich vor dir fürchten, dich zu strafen, und mit dir vor Gericht treten?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Ja, deine Bosheit ist zu groß, und deiner Missetat ist kein Ende.
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Du hast etwa deinem Bruder ein Pfand genommen ohne Ursache, du hast den Nackenden die Kleider ausgezogen;
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
du hast die Müden nicht getränket mit Wasser und hast dem Hungrigen dein Brot versagt;
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
du hast Gewalt im Lande geübet und prächtig drinnen gesessen;
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
die Witwen hast du leer lassen gehen und die Arme der Waisen zerbrochen.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
Darum bist du mit Stricken umgeben, und Furcht hat dich plötzlich erschrecket.
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Solltest du denn nicht die Finsternis sehen, und die Wasserflut dich nicht bedecken?
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Siehe, Gott ist hoch droben im Himmel und siehet die Sterne droben in der Höhe.
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Und du sprichst: Was weiß Gott? Sollt er, das im Dunkeln ist, richten können?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Die Wolken sind seine Vordecke, und siehet nicht, und wandelt im Umgang des Himmels.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Willst du der Welt Lauf achten, darinnen die Ungerechten gegangen sind,
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
die vergangen sind, ehe denn es Zeit war, und das Wasser hat ihren Grund weggewaschen,
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
die zu Gott sprachen: Heb dich von uns, was sollte der Allmächtige ihnen tun können,
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
so er doch ihr Haus mit Gütern füllete? Aber der Gottlosen Rat sei ferne von mir!
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Die Gerechten werden sehen und sich freuen, und der Unschuldige wird ihrer spotten.
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
Was gilt's, ihr Wesen wird verschwinden und ihr Übriges das Feuer verzehren!
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
So vertrage dich nun mit ihm und habe Frieden; daraus wird dir viel Gutes kommen.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Höre das Gesetz von seinem Munde und fasse seine Rede in dein Herz.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Wirst du dich bekehren zu dem Allmächtigen, so wirst du gebauet werden und Unrecht ferne von deiner Hütte tun,
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
so wirst du für Erde Gold geben und für die Felsen güldene Bäche;
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
und der Allmächtige wird dein Gold sein, und Silber wird dir zugehäuft werden.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Dann wirst du deine Lust haben an dem Allmächtigen und dein Antlitz zu Gott aufheben.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
So wirst du ihn bitten, und er wird dich hören; und wirst deine Gelübde bezahlen.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Was du wirst vornehmen, wird er dir lassen gelingen; und das Licht wird auf deinem Wege scheinen.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Denn die sich demütigen, die erhöhet er; und wer seine Augen niederschlägt, der wird genesen.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
Und der Unschuldige wird errettet werden; er wird aber errettet um seiner Hände Reinigkeit willen.