< Yobu 22 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Alors, répondant, Eliphaz, le Thémanite, dit:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Est-ce qu’un homme peut être comparé à Dieu, quand il serait d’une science parfaite?
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Que sert à Dieu que tu sois juste? ou quel bien lui fais-tu si ta voie est sans tache?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Est-ce en craignant qu’il t’accusera, et qu’il viendra avec toi en jugement,
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Et non pas à cause de ta malice très grande et de tes infinies iniquités?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Car tu as retenu le gage de tes frères sans raison, et tu as dépouillé de leurs vêtements ceux qui étaient nus.
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Tu n’as pas donné de l’eau à celui qui était épuisé de lassitude, et à celui qui avait faim tu as soustrait du pain.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Par la force de ton bras tu possédais ta terre, et, étant le plus puissant, tu la conservais.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Tu as renvoyé les veuves les mains vides, et tu as brisé les bras des orphelins.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
C’est pour cela que tu es environné de pièges, et qu’une frayeur soudaine te trouble.
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Et tu pensais que tu ne verrais point de ténèbres, et que tu ne serais pas accablé par un impétueux débordement d’eaux.
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Ne songes-tu pas que Dieu est plus élevé que le ciel, et qu’il est au-dessus du sommet des étoiles?
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Et tu dis: Mais que connaît Dieu? car c’est comme à travers d’une profonde obscurité qu’il juge.
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Des nuées le cachent; il ne considère pas ce qui est de nous, et il parcourt les pôles du ciel.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Est-ce que tu désires suivre le sentier des siècles, qu’ont foulé des hommes iniques,
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
Qui ont été enlevés avant leur temps, et dont un fleuve a renversé le fondement?
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
Qui disaient à Dieu: Retire-toi de nous; et qui estimaient que le Tout-Puissant ne pouvait rien faire;
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Quoique ce fût lui qui eût rempli leurs maisons de biens. Que leur sentiment soit loin de moi!
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Les justes les verront et ils se réjouiront, et l’innocent se moquera d’eux.
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
Est-ce que leur élévation n’a pas été entièrement détruite? et leurs restes, un feu ne les a-t-il pas dévorés?
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Soumets-toi donc à Dieu, et tu auras la paix; et par là tu auras des fruits excellents.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Reçois de sa bouche sa loi, et mets ses discours dans ton cœur.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Si tu reviens au Tout-Puissant, tu seras rétabli, et tu éloigneras l’iniquité de ton tabernacle.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Il te donnera au lieu de terre, un rocher, et au lieu d’un rocher, des torrents d’or.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
Et le Tout-Puissant sera contre tes ennemis, et l’argent sera mis en monceaux pour toi.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Alors tu abonderas en délices dans le Tout-Puissant, et tu élèveras ta face vers Dieu.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Tu le prieras, et il t’exaucera, et tu acquitteras tes vœux.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Tu décideras une chose, et elle se réalisera pour toi, et sur tes voies brillera la lumière.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Car celui qui aura été humilié sera dans la gloire; et celui qui aura baissé les yeux, celui-là même sera sauvé,
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
L’innocent sera sauvé, mais il sera sauvé à cause de la pureté de ses mains.