< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Éliphaz de Théman prit la parole et dit:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Un homme peut-il être utile à Dieu? Non; le sage n’est utile qu’à lui-même.
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Si tu es juste, est-ce à l’avantage du Tout-Puissant? Si tu es intègre dans tes voies, qu’y gagne-t-il?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Est-ce par crainte de toi qu’il te châtie, Qu’il entre en jugement avec toi?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Ta méchanceté n’est-elle pas grande? Tes iniquités ne sont-elles pas infinies?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Tu enlevais sans motif des gages à tes frères, Tu privais de leurs vêtements ceux qui étaient nus;
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Tu ne donnais point d’eau à l’homme altéré, Tu refusais du pain à l’homme affamé.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Le pays était au plus fort, Et le puissant s’y établissait.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Tu renvoyais les veuves à vide; Les bras des orphelins étaient brisés.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
C’est pour cela que tu es entouré de pièges, Et que la terreur t’a saisi tout à coup.
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Ne vois-tu donc pas ces ténèbres, Ces eaux débordées qui t’envahissent?
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Dieu n’est-il pas en haut dans les cieux? Regarde le sommet des étoiles, comme il est élevé!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Et tu dis: Qu’est-ce que Dieu sait? Peut-il juger à travers l’obscurité?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Les nuées l’enveloppent, et il ne voit rien; Il ne parcourt que la voûte des cieux.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Eh quoi! Tu voudrais prendre l’ancienne route Qu’ont suivie les hommes d’iniquité?
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
Ils ont été emportés avant le temps, Ils ont eu la durée d’un torrent qui s’écoule.
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
Ils disaient à Dieu: Retire-toi de nous; Que peut faire pour nous le Tout-Puissant?
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Dieu cependant avait rempli de biens leurs maisons. Loin de moi le conseil des méchants!
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Les justes, témoins de leur chute, se réjouiront, Et l’innocent se moquera d’eux:
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
Voilà nos adversaires anéantis! Voilà leurs richesses dévorées par le feu!
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Attache-toi donc à Dieu, et tu auras la paix; Tu jouiras ainsi du bonheur.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Reçois de sa bouche l’instruction, Et mets dans ton cœur ses paroles.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Tu seras rétabli, si tu reviens au Tout-Puissant, Si tu éloignes l’iniquité de ta tente.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Jette l’or dans la poussière, L’or d’Ophir parmi les cailloux des torrents;
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
Et le Tout-Puissant sera ton or, Ton argent, ta richesse.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Alors tu feras du Tout-Puissant tes délices, Tu élèveras vers Dieu ta face;
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Tu le prieras, et il t’exaucera, Et tu accompliras tes vœux.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
A tes résolutions répondra le succès; Sur tes sentiers brillera la lumière.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Vienne l’humiliation, tu prieras pour ton relèvement: Dieu secourt celui dont le regard est abattu.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
Il délivrera même le coupable, Qui devra son salut à la pureté de tes mains.

< Yobu 22 >