< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Alors Éliphaz, le Thémanite, prit la parole,
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
« Un homme peut-il être utile à Dieu? Certes, celui qui est sage est profitable à lui-même.
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Est-ce un plaisir pour le Tout-Puissant que vous soyez justes? Ou est-ce que ça lui profite que vous rendiez vos voies parfaites?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Est-ce pour votre piété qu'il vous réprimande, qu'il entre avec vous dans le jugement?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Votre méchanceté n'est-elle pas grande? Il n'y a pas non plus de fin à vos iniquités.
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Car tu as pris des gages de ton frère pour rien, et ont dépouillé les nus de leurs vêtements.
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Vous n'avez pas donné d'eau à boire à ceux qui sont fatigués, et vous avez refusé du pain aux affamés.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Mais le puissant, lui, avait la terre. L'homme honorable, il y a vécu.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Tu as renvoyé les veuves à vide, et les bras de l'orphelin ont été brisés.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
C'est pourquoi il y a des pièges autour de toi. Une peur soudaine vous trouble,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
ou l'obscurité, de sorte que vous ne pouvez pas voir, et des flots d'eaux te couvrent.
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
« Dieu n'est-il pas dans les hauteurs du ciel? Voyez la hauteur des étoiles, comme elles sont hautes!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
Vous dites: « Que sait Dieu? Peut-il juger à travers l'obscurité épaisse?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Des nuages épais le couvrent, de sorte qu'il ne voit pas. Il marche sur la voûte du ciel.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Garderez-vous l'ancienne manière, que les hommes méchants ont foulés,
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
qui ont été enlevés avant leur heure, dont le fondement a été déversé comme un torrent,
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
qui ont dit à Dieu: « Eloigne-toi de nous ». et « Que peut faire le Tout-Puissant pour nous? ».
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Pourtant, il a rempli leurs maisons de bonnes choses, mais le conseil des méchants est loin de moi.
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Les justes le voient et se réjouissent. Les innocents les ridiculisent,
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
en disant: « Ceux qui se sont élevés contre nous ont été exterminés. Le feu a consumé leur reste.
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
« Fais connaissance avec lui maintenant, et sois en paix. Par elle, le bien viendra à toi.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Veuillez recevoir l'instruction de sa bouche, et déposez ses paroles dans votre cœur.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Si vous revenez au Tout-Puissant, vous serez édifiés, si vous éloignez l'iniquité loin de vos tentes.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Dépose ton trésor dans la poussière, l'or d'Ophir parmi les pierres des ruisseaux.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
Le Tout-Puissant sera ton trésor, et de l'argent précieux pour vous.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Car alors tu te complairas dans le Tout-Puissant, et tu lèveras ton visage vers Dieu.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Tu le prieras, et il t'écoutera. Tu paieras tes vœux.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Tu décréteras aussi une chose, et elle sera établie pour toi. La lumière brillera sur vos chemins.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Lorsqu'ils s'abaisseront, tu diras: « Relève-toi ». Il sauvera l'humble personne.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
Ildélivrera même celui qui n'est pas innocent. Oui, il sera délivré par la propreté de vos mains. »

< Yobu 22 >